Saturday, June 23, 2007

NDINGATHE BWANJI?

Chewa


Macitidwe 8: 26-40

26. Koma mngelo wa Ambuye analankhula ndi Filipo, nanena, Nyamuka, nupite mbali ya kumwela, kutsata njira yotsikakucokera ku Yerusalemu kunka ku Gaza; ndiyo ya cipululu.
27. Ndipo ananyamuka napita; ndipo taona munthu waku Aitiopiya, mdindo wamphamvu wa Kandake, mfumu yaikazi ya Aaitiopiya, ndiye wakusunga cuma cace conse, amene anadza ku Yerusalemu kudzapemphera;
28. Ndipo analinkubwerera, nalikukhala pa gareta wace, nawerenga mneneri Yesaya.
29. Ndipo Mzimu anati kwa Filipo, Yandikira, nudziphatike ku gareta uyu.
30. Ndipo Filipo anamthamangira, namva iye alikuwerenga Yesaya mneneri, ndipo anati, Kodi muzindikira cimene muwerenga?
31. Koma anati, Ndingathe bwanji, popanda munthu wonditsogolera ine? ndipo anapempha Filipo akwere nakhale naye.
32. Koma palembo pamene analikuwerengapo ndipo,
Ngati nkhosa anatengedwa kukaphedwa,
Ndi monga mwana wa nkhosa ali du pamaso pa womsenga,
Kotero sanatsegula pakamwa pace:
33. M’kucepetsedwa kwace ciweruzo cace cinacotsedwa;
Mbadwo wace adzaubukitsa ndani?
Cifukwa wacotsedwa kudziko moyo wace.
34. Ndipo mdindoyo anayankha Filipo, nati Ndikupempha, mneneri anena ici za yani? za yekha, kapena za wina?
35. Ndipo Filipo anatsegula pakamwa pace, nayamba pa lembo ili, nalalikira kwa iye Yesu.
36. Ndipo monga panpita pao, anadza ku madzi akuti; ndipo mdindoyo anati, Taonapo madzi; cindiletsa ine ciani ndisabatiziwe?
38. Ndipo anamuuza kuti aimitse gareta; ndipo anatsikira onse awiri kumadzi, Filipo ndi mdindoyo; ndipo anambatiza iye.
39. Ndipo pamene anakwera kuturuka m’madzi, Mzimu wa Ambuye anakwatula Filipo; ndipo mdindo sanamuonanso, pakuti anapita njira yace wokondwera.
40. Koma Filipo anapezedwa ku Azotu; ndipo popitapita analalikira Uthenga Wabwino m’midzi yonse, kufikira anadza iye ku Kaisareya.

No comments: